Categories
1 YOHANE

1 YOHANE 1

Mau a moyo aoneka m’thupi

1 Chimene chinaliko kuyambira pachiyambi, chimene tidachimva, chimene tidachiona m’maso mwathu, chimene tidachipenyerera, ndipo manja athu adachigwira cha Mau a moyo,

2 (ndipo moyowo unaonekera, ndipo tidaona, ndipo tichita umboni, ndipo tikulalikirani moyo wosathawo, umene unali kwa Atate, nuonekera kwa ife);

3 chimene tidachiona, ndipo tidachimva, tikulalikirani inunso, kuti inunso mukayanjane pamodzi ndi ife; ndipo chiyanjano chathu chilinso ndi Atate, ndipo ndi Mwana wake YesuKhristu;

4 ndipo izi tilemba ife, kuti chimwemwe chathu chikwaniridwe.

Mulungu ali kuunika; wosayenda m’kuunika alibe chiyanjano ndi Iye

5 Ndipo uwu ndi uthenga tidaumva kwa Iye, ndipo tiulalikira kwa inu, kuti Mulungu ndiye kuunika, ndipo mwa Iye monse mulibe mdima.

6 Tikati kuti tiyanjana ndi Iye, ndipo tiyenda mumdima, tinama, ndipo sitichita choonadi;

7 koma ngati tiyenda m’kuunika, monga Iye ali m’kuunika, tiyanjana wina ndi mnzake, ndipo mwazi wa Yesu Mwana wake utisambitsa kutichotsera uchimo wonse.

Za kuwulula machimo ndi kukhululukidwa

8 Tikati kuti tilibe uchimo, tidzinyenga tokha, ndipo mwa ife mulibe choonadi.

9 Ngati tivomereza machimo athu, ali wokhulupirika ndi wolungama Iye, kuti atikhululukire machimo athu, ndi kutisambitsa kutichotsera chosalungama chilichonse.

10 Tikanena kuti sitidachimwe, timuyesa Iye wonama, ndipo mau ake sakhala mwa ife.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1JN/1-fa5d2d29720872ba878eb0893245f4ae.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *