Pemphero la kwa anthu onse
1 Ndidandaulira tsono, poyambayamba, kuti achitike mapembedzo, mapemphero, mapembedzero, mayamiko, chifukwa cha anthu onse;
2 chifukwa cha mafumu ndi onse akuchita ulamuliro; kuti m’moyo mwathu tikakhale odika mtima ndi achete m’kulemekeza Mulungu, ndi m’kulemekezeka monse.
3 Pakuti ichi nchokoma ndi cholandirika pamaso pa Mulungu Mpulumutsi wathu;
4 amene afuna anthu onse apulumuke, nafike pozindikira choonadi.
5 Pakuti pali Mulungu mmodzi, ndi Mtetezi mmodzi pakati pa Mulungu ndi anthu, ndiye munthu,KhristuYesu,
6 amene anadzipereka yekha chiombolo m’malo mwa onse; umboni m’nyengo zake;
7 umene anandiika ine mlaliki wake ndimtumwi(ndinena zoona, wosanama ine), mphunzitsi waamitundum’chikhulupiriro ndi choonadi.
8 Chifukwa chake ndifuna kuti amunawo apemphere pamalo ponse, ndi kukweza manja oyera, opanda mkwiyo ndi makani.
Zoyenera akazi
9 Momwemonso, akazi adziveke okha ndi chovala choyenera, ndi manyazi, ndi chidziletso; osati ndi tsitsi lake loluka, ndi golide kapena ngale, kapena malaya a mtengo wake wapatali;
10 komatu (umo mokomera akazi akuvomereza kulemekeza Mulungu), mwa ntchito zabwino.
11 Mkazi aphunzire akhale wachete m’kumvera konse.
12 Koma sindilola ine kuti mkazi aphunzitse, kapena kulamulira mwamuna; komatu akhale chete.
13 PakutiAdamuanayamba kulengedwa, pamenepo Heva;
14 ndipo Adamu sananyengedwe, koma mkaziyo ponyengedwa analowa m’kulakwa;
15 koma adzapulumutsidwa mwa kubala mwana, ngati akhala m’chikhulupiriro ndi chikondi ndi chiyeretso pamodzi ndi chidziletso.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1TI/2-0a8170af0d1cfbfedbd854c5012a08a6.mp3?version_id=1068—