Categories
1 PETRO

1 PETRO Mau Oyamba

Mau Oyamba

Kalata yoyamba ya Petro

analembera Akhristu, amene panopa akutchedwa “anthu osankhika a Mulungu”, amene anabalalika m’dera lonse la dziko limene masiku ano limatchedwa Turkey. Cholinga chenicheni cha kalatayi ndicho kuwalimbikitsa owerengawo, amene amakumana ndi mazunzo osiyanasiyana ndipo amasautsidwa chifukwa cha chikhulupiriro chao. Olembayo akuchita izi powakumbutsa awerengiwo za Uthenga Wabwino wa Yesu Khristu umene imfa yake, kuuka kwake ndi lonjezano la kubweranso kwake, zinawapatsa chiyembekezo. Chifukwa chake iwowa ayenera kuvomereza zakuti adzazunzika ndipo apirire m’masautso. Iwo atsimikizike kuti kuzunzidwaku ndiko mayeso a kulimba kwa chikhulupiriro chao ndipo adzalandira mphotho “pa vumbulutso la Yesu Khristu” (1.7).

Kuphatikizapo chilimbikitso chimenechi m’nthawi ya mazunzo, olembayo akuwalimbikitsa awerengi ake kuti akhale m’moyo monga anthu amene ali ake a Khristu.

Za mkatimu

Mau oyamba 1.1-2

Kukumbutsa za chipulumutso cha Mulungu 1.3-12

Kulimbikitsana za khalidwe la moyo woyera 1.13—2.10

Udindo wa Mkhristu pa nthawi ya mazunzo 2.11—4.19

Kudzichepetsa ndi utumiki wa Chikhristu 5.1-11

Mau omaliza 5.12-14

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *