Mau Oyamba
Mabuku awiri otchedwa
Mbiri
akambanso zina ndi zina zimene zidakambidwa kale m’mabuku a
Samuele
ndi a
Mafumu
; koma kakambidwe kake nkosiyaniranapo polongosola mbiri ya ufumu wa Israele, chifukwa olemba mabuku a
Mbiri
ali ndi zolinga ziwiri:
1. Afuna kuwonetsa kuti, ngakhale Israele ndi a Yuda adawonongeka kotheratu, Mulungu salephera kuchita zimene analonjeza, mwakuti akuwongolerabe zinthu kudzera mwa anthu okhala mu Yuda, monga momwe adaziganiziratu pa chiyambi. Pofuna kulimbikitsa chiyembekezo chimenechi, olemba mabukuwa akukumbutsa zazikulu zimene adachita Davide ndi Solomoni, ndiponso ntchito za Yehosafati, Hezekiya ndi Yosiya, zothandiza anthu kukhala okhulupirika kwa Mulungu.
2. Afunanso kulongosola za chiyambi cha chipembedzo mu Kachisi wa Yehova ku Yerusalemu, ndiponso za udindo wa ansembe ndi Alevi pa mwambo wa chipembedzo. M’mabuku awiriwo Davide akuwoneka kuti iye ndi mkulu woyambitsa zonsezi, ngakhale amene anamanga Kachisi wa Yehova anali Solomoni.
Buku loyamba la
Mbiri
lifotokoza makamaka za ufumu wa Davide.
Za mkatimu
Mndandanda wa anthu akale ndiponso wa makolo a Israele
1.1—9.44
Imfa ya Saulo
10.1-14
Ufumu wa Davide
11.1—29.30
a. Mavuto ake ndipo ntchito za zazikulu
11.1—22.1
b. Zokonzekera kumanga Kachisi wa Yehova
22.2—29.30