Adzukulu a Benjamini ndi Saulo
1 Ndipo Benjamini anabala Bela mwana wake woyamba, Asibele wachiwiri, ndi Ahara wachitatu,
2 Noha wachinai, ndi Rafa wachisanu.
3 Ndi Bela anali ndi ana: Adara, ndi Gera, ndi Abihudi,
4 ndi Abisuwa, ndi Naamani, ndi Ahowa,
5 ndi Gera, ndi Sefufani, ndi Huramu.
6 Ndi ana a Ehudi ndi awa: ndiwo akulu a nyumba za makolo ao a iwo okhala ku Geba, ndipo anawatenga ndende kunka ku Manahati,
7 natenga ndende Naamani, ndi Ahiya, ndi Gera, ndipo, anabala Uza, ndi Ahihudi.
8 Ndipo Saharaimu anabala ana ku dziko la Mowabu, atachotsa akazi ake Husimu ndi Baara.
9 Ndipo Hodesi mkazi wake anambalira Yobabu, ndi Zibiya, ndi Mesa, ndi Malikamu,
10 ndi Yeuzi, ndi Sakiya, ndi Mirima. Awa ndi ana ake aakulu a nyumba za makolo ao.
11 Ndi Husimu anambalira Abitubu, ndi Elipaala.
12 Ndi ana a Elipaala: Eberi, ndi Misamu, ndi Semedi, amene anamanga Ono, ndi Lodi ndi midzi yake,
13 ndi Beriya, ndi Sema; ndiwo akulu a nyumba za makolo a iwo okhala mu Ayaloni, amene anathawitsa okhala mu Gati;
14 ndi Ahiyo, Sasaki, ndi Yeremoti,
15 ndi Zebadiya, ndi Aradi, ndi Edere,
16 ndi Mikaele, ndi Isipa, ndi Yoha, ana a Beriya;
17 ndi Zebadiya, ndi Mesulamu, ndi Hiziki, ndi Hebere,
18 ndi Isimerai, ndi Iziliya, ndi Yobabu, ana a Elipaala;
19 ndi Yakimu, ndi Zikiri, ndi Zabidi,
20 ndi Eliyenai, ndi Ziletai, ndi Eliyele,
21 ndi Adaya, ndi Beraya, ndi Simiratu, ana a Simei;
22 ndi Isipani, ndi Eberi, ndi Eliyele,
23 ndi Abidoni, ndi Zikiri, ndi Hanani,
24 ndi Hananiya, ndi Elamu, ndi Antotiya,
25 ndi Ifidea, ndi Penuwele, ana a Sasaki;
26 ndi Samuserai, ndi Sehariya, ndi Ataliya,
27 ndi Yaaresiya ndi Eliya, ndi Zikiri, ana a Yerohamu.
28 Awa ndi akulu a nyumba za makolo mwa mibadwo yao, ndiwo akulu anakhala muYerusalemuawa.
29 Ndipo mu Gibiyoni anakhala atate a Gibiyoni, dzina la mkazi wake ndiye Maaka;
30 ndi mwana wake woyamba ndiye Abidoni, opondana naye ndi Zuri, ndi Kisi, ndi Baala, ndi Nadabu,
31 ndi Gedori, ndi Ahiyo, ndi Zekeri.
32 Ndipo Mikiloti anabala Simea. Ndi iwonso anakhala pamodzi ndi abale ao mu Yerusalemu, popenyana ndi abale ao.
33 Ndipo Nere anabala Kisi, ndi Kisi anabala Saulo, ndi Saulo anabala Yonatani, ndi Malikisuwa, ndi Abinadabu, ndi Esibaala.
34 Ndi mwana wa Yonatani, ndiye Meribaala; ndi Meribaala anabala Mika.
35 Ndi ana a Mika: Pitoni, ndi Meleki, ndi Tareya, ndi Ahazi.
36 Ndi Ahazi anabala Yehoyada, ndi Yehoyada anabala Alemeti, ndi Azimaveti, ndi Zimiri; ndi Zimiri anabala Moza;
37 ndi Moza anabala Bineya, mwana wake ndiye Rafa, mwana wake Eleasa, mwana wake Azele;
38 ndipo Azele anali nao ana asanu ndi mmodzi, maina ao ndiwo Azirikamu, Bokeru, ndi Ismaele, ndi Seyariya, ndi Obadiya, ndi Hanani. Onsewa ndiwo ana a Azele.
39 Ndipo ana a Eseki mbale wake: Ulamu mwana wake woyamba, Yeusi wachiwiri, ndi Elifeleti wachitatu.
40 Ndipo ana a Ulamu ndiwo ngwazi zamphamvu, ndiwo oponya mivi, nakhala nao ana ambiri ndi zidzukulu zana limodzi. Onsewa ndiwo a ana a Benjamini.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1CH/8-8eb82e0f6e5539828723bda2608c89df.mp3?version_id=1068—