Categories
1 MBIRI

1 MBIRI 3

Adzukulu a Davide

1 Ana a Davide tsono ombadwira ku Hebroni: woyamba Aminoni wa Ahinowamu wa ku Yezireele, wachiwiri Daniele wa Abigaile wa ku Karimele,

2 wachitatu Abisalomu mwana wa Maaka mwana wamkazi wa Talimai mfumu ya Gesuri, wachinai Adoniya mwana wa Hagiti,

3 wachisanu Sefatiya wa Abitala, wachisanu ndi chimodzi Itireamu wa mkazi wake Egila.

4 Anambadwira asanu ndi mmodzi mu Hebroni; ndi pomwepo anakhala mfumu zaka zisanu ndi ziwiri, ndi miyezi isanu ndi iwiri; ndi muYerusalemuanakhala mfumu zaka makumi atatu mphambu zitatu.

5 Ndipo ombadwira mu Yerusalemu ndi awa: Simea, ndi Sobabu, ndi Natani, ndi Solomoni, anai a Batisuwa mwana wamkazi wa Amiyele;

6 ndi Ibara, ndi Elisama, ndi Elifeleti,

7 ndi Noga, ndi Nefegi, ndi Yafiya,

8 ndi Elisama, ndi Eliyada, ndi Elifeleti, asanu ndi anai.

9 Onsewa ndiwo ana a Davide, pamodzi ndi ana a akazi aang’ono; ndipo Tamara ndiye mlongo wao.

10 Ndipo mwana wa Solomoni ndiye Rehobowamu, Abiya mwana wake, Asa mwana wake, Yehosafati mwana wake,

11 Yoramu mwana wake, Ahaziya mwana wake, Yowasi mwana wake,

12 Amaziya mwana wake, Azariya mwana wake, Yotamu mwana wake,

13 Ahazi mwana wake, Hezekiya mwana wake, Manase mwana wake,

14 Amoni mwana wake, Yosiya mwana wake.

15 Ndi ana a Yosiya: woyamba Yohanani, wachiwiri Yehoyakimu, wachitatu Zedekiya, wachinai Salumu.

16 Ndi ana a Yehoyakimu: Yekoniya mwana wake, Zedekiya mwana wake.

17 Ndi mwana wa Yekoniya: Asiri, Sealatiele mwana wake,

18 ndi Malikiramu, ndi Pedaya, ndi Senazara, Yekamiya, Hosama, Nedabiya.

19 Ndi ana a Pedaya: Zerubabele ndi Simei; ndi ana a Zerubabele: Mesulamu, ndi Hananiya; ndipo Selomiti ndiye mlongo wao,

20 ndi Hasuba, ndi Ohele, ndi Berekiya, ndi Hasadiya, ndi Yusabu-hesede; asanu.

21 Ndi ana a Hananiya: Pelatiya, ndi Yesaya, ana a Refaya, ana a Arinani, ana a Obadiya, ana a Sekaniya.

22 Ndi mwana wa Sekaniya: Semaya; ndi ana a Semaya: Hatusi, ndi Igala, ndi Bariya, ndi Neariya, ndi Safati; asanu ndi mmodzi.

23 Ndi ana a Neariya: Eliyoenai, ndi Hizikiya, ndi Azirikamu, atatu.

24 Ndi ana a Eliyoenai: Hodaviya, ndi Eliyasibu, ndi Pelaya, ndi Akubu, ndi Yohanani, ndi Delaya, ndi Anani, asanu ndi awiri.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1CH/3-e0b322d726dde0d04c198480c0f34a2f.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *