1 Ndipo kunali, pofikanso chaka, nyengo yakutuluka mafumu, Yowabu anatsogolera khamu lamphamvu, napasula dziko la ana a Amoni, nadza, naumangira misasa Raba. Koma Davide anakhala kuYerusalemu. Ndipo Yowabu anakantha Raba, naupasula.
2 Ndipo Davide anatenga korona wa mfumu yao kumchotsa pamutu pake, napeza kulemera kwake talente wa golide; panalinso miyala ya mtengo wake pamenepo; ndipo anamuika pamutu pa Davide, natulutsa zankhondo za m’mzindamo zambiri ndithu.
3 Natulutsanso anthu anali m’mwemo, nawacheka ndi mipeni ya manomano, ndi zipangizo zochekera zachitsulo, ndi nkhwangwa. Anatero Davide ndi mizinda yonse ya ana a Amoni. Ndipo Davide ndi anthu onse anabwera ku Yerusalemu.
Abwereza kukantha Afilisti
4 Ndipo zitatha izi, inauka nkhondo ku Gezere ndi Afilisti; pamenepo Sibekai Muhusa anapha Sipai wa ana a chimphona; ndipo anawagonjetsa.
5 Ndipo panalinso nkhondo ndi Afilisti; ndi Elihanani mwana wa Yairi anapha Lami mbale wa Goliyati Mgiti, amene luti la mkondo wake linanga mtanda woombera nsalu.
6 Ndipo panalinso nkhondo ku Gati; kumeneko kunali munthu wa msinkhu waukulu, amene zala zake za kumanja ndi kumapazi ndizo makumi awiri mphambu zinai; zisanu ndi chimodzi ku dzanja lililonse, ndi zisanu ndi chimodzi ku phazi lililonse; nayenso anabadwa mwa chimphonacho.
7 Ndipo potonza Israele iyeyu Yonatani mwana wa Simea mbale wake wa Davide anamkantha.
8 Awa anabadwa mwa chimphonacho ku Gati, koma anagwa ndi dzanja la Davide ndi la anyamata ake.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1CH/20-1a6920d4244cba0897aec2a6b17e5b50.mp3?version_id=1068—