Ahabu apangana ndi Yehosafati
1 Ndipo Aaramu ndi Aisraele anakhala chete zaka zitatu, osathirana nkhondo.
2 Koma kunachitika chaka chachitatu, kuti Yehosafati mfumu ya Yuda anatsikira kwa mfumu ya Israele.
3 Ndipo mfumu ya Israele ananena ndi anyamata ake, nati, Kodi simudziwa kuti Ramoti Giliyadi ngwathu, ndipo tangokhala chete, osaulanditsa m’dzanja la mfumu ya Aramu.
4 Tsono anati kwa Yehosafati, Kodi udzapita nane kunkhondo ku Ramoti Giliyadi? Ndipo Yehosafati anati kwa mfumu ya Israele, M’mene ukhalira iwe ndi momwe ndikhalira ndine; anthu anga monga anthu ako, akavalo anga monga akavalo ako.
5 Ndipo Yehosafati ananena ndi mfumu ya Israele, Funsira ku mau a Yehova lero.
6 Pamenepo mfumu ya Israele inasonkhanitsa aneneri ngati anthu mazana anai, nanena nao, Kodi ndizimuka kukathira nkhondo pa Ramoti Giliyadi, kapena ndileke? Nati iwo, Kweraniko; popeza Ambuye adzaupereka m’dzanja la mfumu.
7 Koma Yehosafati anati, Kodi pano palibemneneriwina wa Yehova, kuti tifunsire kwa iye?
8 Ndipo mfumu ya Israele inati kwa Yehosafati, Alipo munthu wina kuti tifunsire kwa Yehova mwa iye; koma ndimuda, popeza samanenera za ine zabwino, koma zoipa; ndiye Mikaya mwana wake wa Imila. Nati Yehosafati, Isamatero mfumu.
9 Tsono mfumu ya Israele anaitana mdindo, nati, Kamtenge msanga Mikaya mwana wa Imila.
10 Ndipo mfumu ya Israele ndi Yehosafati mfumu ya Yuda anakhala onse awiri, yense pa mpando wachifumu wake, ovala zovala zao zachifumu pabwalo popondera mphesa pa khomo la chipata cha Samariya; ndipo aneneri onse ananenera pamaso pao.
11 Ndipo Zedekiya mwana wa Kenana anadzisulira nyanga zachitsulo, nati, Atero Yehova, Ndi izi mudzagunda nazo Aaramu mpaka atatha psiti.
12 Ndipo aneneri onse ananena momwemo, nati, Kwerani ku Ramoti Giliyadi, ndipo mudzachita mwai; popeza Yehova adzaupereka m’dzanja la mfumu.
Mikaya anenera motsutsa Ahabu
13 Tsono mthenga uja udakaitana Mikaya unanena naye, nati, Taona, mau a aneneri avomerezana zokoma kwa mfumu ndi m’kamwa mmodzi; mau ako tsono afanane ndi mau a wina wa iwowo, nunene zabwino.
14 Koma Mikaya anati, Pali Yehova, zimene Yehova adzanena nane ndidzanena ine.
15 Ndipo atafika kwa mfumu, mfumu inati kwa iye, Mikaya, kodi tizimuka ku Ramoti Giliyadi kukathira nkhondo, kapena tileke? Nati iye, Kwerani, ndipo mudzachita mwai, popeza Yehova adzaupereka m’dzanja la mfumu.
16 Ndipo mfumu inati, Ndikulumbiritse kangati kuti undiuze zoona zokhazokha m’dzina la Yehova?
17 Nati iye, Ndinaona Aisraele onse obalalika pamapiri ngati nkhosa zopanda mbusa; ndipo Yehova anati, Izi zilibe mwini, yense abwerere ndi mtendere kunyumba yake.
18 Pamenepo mfumu ya Israele inanena ndi Yehosafati, Kodi sindinakuuze kuti uyu sadzanenera za ine zabwino, koma zoipa?
19 Ndipo anati, Chifukwa chake tamverani mau a Yehova, Ndinaona Yehova alikukhala pa mpando wake wachifumu, ndi khamu lonse lakumwamba lili chilili m’mbali mwake, ku dzanja lamanja ndi lamanzere.
20 Nati Yehova, Adzanyenga Ahabu ndani, kuti akwere nagwe ku Ramoti Giliyadi? Ndipo anati wina mwakuti, wina mwakuti.
21 Pamenepo mzimu wina unatuluka, nuima pamaso pa Yehova, nuti, Ndidzamnyenga ndine. Nati Yehova kwa iye, Motani?
22 Nati, Ndidzatuluka, ndidzakhala mzimu wonama m’kamwa mwa aneneri ake onse. Nati, Udzamnyengadi, nudzakhozanso; tuluka, ukatero kumene.
23 Ndipo tsopano taonani, Yehova waika mzimu wonama m’kamwa mwa aneneri anu onse awa, ndipo Yehova ananena choipa cha inu.
24 Pamenepo Zedekiya mwana wa Kenana anasendera, napanda Mikaya patsaya, nati, Mzimu wa Yehova wandichokera bwanji, kulankhula ndi iwe?
25 Mikaya nati, Taona, udzapenya tsiku lolowa iwe m’chipinda cha pakati kubisala.
26 Pamenepo inati mfumu ya Israele, Tengani Mikaya, mumbweze kwa Amoni kalonga wa mzinda, ndi kwa Yowasi mwana wa mfumu;
27 ndipo muziti, Itero mfumu, Khazikani uyu m’kaidi, mumdyetse chakudya cha nsautso, ndi madzi a nsautso, mpaka ndikabwera ndi mtendere.
28 Ndipo Mikaya anati, Mukabwera ndithu ndi mtendere Yehova sanalankhule mwa ine. Nati, Mvetsani, anthu inu nonse.
Ahabu aphedwa mu nkhondo ya pa Aramu
29 Tsono mfumu ya Israele ndi Yehosafati mfumu ya Yuda anakwera ku Ramoti Giliyadi.
30 Ndipo mfumu ya Israele inanena ndi Yehosafati, Ine ndidzadzizimbaitsa, ndi kulowa kunkhondo, koma vala iwe zovala zako zachifumu. Ndipo mfumu ya Israele inadzizimbaitsa, nilowa kunkhondo.
31 Tsono mfumu ya Aramu idalamulira akapitao makumi atatu mphambu ziwiri za magaleta ake, niti, Musaponyana ndi anthu aang’ono kapena aakulu, koma ndi mfumu ya Israele yokha.
32 Ndipo kunali, akapitao a magaleta ataona Yehosafati, anati, Zedi uyu ndiye mfumu ya Israele imene, napotolokera kukaponyana naye; koma Yehosafati anafuula.
33 Ndipo pamene akapitao a magaleta anaona kuti sindiye mfumu ya Israele, anabwerera osampirikitsa.
34 Ndipo munthu anakoka uta wake chiponyeponye, nalasa mfumu ya Israele pakati pa maluma a malaya achitsulo; tsono ananena ndi mnyamata wa galeta wake, Tembenuza dzanja lako, nundichotse kunkhondo, popeza ndalasidwa.
35 Ndipo nkhondo inakula tsiku lomwelo, ndipo mfumu inagwirizidwa m’galeta mwake kupenyana ndi Aaramu, natsirizika madzulo; ndipo mwazi unatuluka m’bala pa phaka la galeta.
36 Ndipo mfuu unafikira khamu lonse la nkhondo polowa dzuwa, ndi kuti, Yense kumzinda kwao, ndi yense ku dziko la kwao.
37 Ndipo inafa mfumu, naifikitsa ku Samariya, naika mfumu mu Samariya.
38 Ndipo potsuka galetayo pa thawale la ku Samariya agalu ananyambita mwazi wake, paja pamasamba akazi adama, monga mwa mau a Yehova amene ananenawo.
39 Tsono machitidwe ena a Ahabu, ndi zonse adazichita, ndi nyumba ya minyanga adaimanga, ndi mizinda yonse adaimanga, sizinalembedwe kodi m’buku la machitidwe a mafumu a Israele?
40 Ndipo Ahabu anagona ndi makolo ake; ndi Ahaziya mwana wake anakhala mfumu m’malo mwake.
Yehosafati mfumu ya Yuda
41 Koma Yehosafati mwana wa Asa anayamba kukhala mfumu ya Yuda chaka chachinai cha Ahabu mfumu ya Israele.
42 Yehosafati anali wa zaka makumi atatu mphambu zisanu, pamene analowa ufumu, nakhala mfumu zaka makumi awiri mphambu zisanu muYerusalemu. Ndi dzina la amake linali Azuba mwana wa Sili.
43 Ndipo anayenda m’njira yonse ya atate wake Asa, osapatukamo; nachita choyenera pamaso pa Yehova, koma misanje sanaichotse; anthu anapherabe nsembe, nafukiza zonunkhira pamsanje.
44 Ndipo Yehosafati anachitana mtendere ndi mfumu ya Israele.
45 Tsono machitidwe ena a Yehosafati, ndi mphamvu anaionetsayo, ndi umo anathira nkhondo, sizinalembedwe kodi m’buku la machitidwe a mafumu a Yuda?
46 Ndipo anachotsa m’dziko anyamata onyansa aja adatsalira masiku a atate wake Asa.
47 Ndipo mu Edomu munalibe mfumu, koma kazembe wa mfumu.
48 Yehosafati anamanga zombo za ku Tarisisi kukatenga golide ku Ofiri; koma sizinamuke, popeza zinaphwanyika pa Eziyoni-Gebere.
49 Pamenepo Ahaziya mwana wa Ahabu ananena ndi Yehosafati, Anyamata anga amuke pamodzi ndi anyamata anu m’zombo. Koma Yehosafati anakana.
50 Ndipo Yehosafati anagona ndi makolo ake, naikidwa ndi makolo ake m’mzinda wa Davide kholo lake; ndipo Yehoramu mwana wake anakhala mfumu m’malo mwake.
Ahaziya mfumu Israele
51 Ahaziya mwana wa Ahabu anayamba kukhala mfumu ya Israele pa Samariya m’chaka chakhumi mphambu zisanu ndi ziwiri cha Yehosafati mfumu ya Yuda; nakhala mfumu ya Israele zaka ziwiri.
52 Nachita choipa pamaso pa Yehova, nayenda m’njira ya atate wake, ndi ya amake, ndi ya Yerobowamu mwana wa Nebati, amene adachimwitsa Israele.
53 NatumikiraBaala, namweramira, naputa mkwiyo wa Yehova Mulungu wa Israele, monga umo anachitira atate wake.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1KI/22-9f1097c9a2d8df5e1ab4d1ed3bbfede1.mp3?version_id=1068—