Categories
1 MAFUMU

1 MAFUMU 19

Eliya athawa Yezebele

1 Ndipo Ahabu anauza Yezebele zonse anazichita Eliya, ndi m’mene anawaphera ndi lupanga aneneri onsewo.

2 Tsono Yezebele anatuma mthenga kwa Eliya, wakuti, Milungu indilange nionjezepo, ngati sindilinganiza moyo wako ndi moyo wa mmodzi wa iwowo mawa nthawi yomwe ino.

3 Ndipo iye ataona chimenechi, ananyamuka, nathawa kupulumutsa moyo, nafika ku Beereseba wa ku Yuda, nasiya mnyamata wake pamenepo.

4 Koma iye mwini analowa m’chipululu ulendo wa tsiku limodzi, nakakhala pansi patsinde pa mtengo watsanya, napempha kuti afe; nati, Kwafikira, chotsani tsopano moyo wanga, Yehova; popeza sindili wokoma woposa makolo anga.

5 Ndipo anagona tulo patsinde pa mtengo watsanya; ndipo taonani, wamthenga anamkhudza, nati kwa iye, Uka nudye.

6 Ndipo anacheuka, naona kumutu kunali kamkate kootcha pamakala, ndi mkhate wa madzi. Tsono anadya namwa, nagonanso pansi.

7 Ndipo mthenga wa Yehova anafikanso kachiwiri, namkhudza, nati, Tauka, idya, popeza ulendo udzakukanika.

8 Tsono anauka, nadya namwa, nayenda ndi mphamvu ya chakudya chimenecho masiku makumi anai usana ndi usiku, nafika kuphiri la Mulungu ku Horebu.

Eliya kuphiri la Horebu

9 Nafika kuphanga, nagona kumeneko, ndipo taonani, mau a Yehova anamfikira, nati kwa iye, Uchitanji pano, Eliya?

10 Ndipo anati, Ine ndinachitira changu Yehova Mulungu wa makamu; popeza ana a Israele anasiyachipanganochanu, napasula maguwa anu a nsembe, napha aneneri anu ndi lupanga, ndipo ndatsala ndekha, ndipo afuna moyo wanga kuuchotsa.

11 Ndipo Iye anati, Tuluka, nuime paphiri lino pamaso pa Yehova. Ndipo taonani, Yehova anapitapo, ndi mphepo yaikulu ndi yamphamvu inang’amba mapiri, niphwanya matanthwe pamaso pa Yehova; koma Yehova sanakhale m’mphepomo. Itapita mphepoyo kunali chivomezi; komanso Yehova sanali m’chivomezicho.

12 Chitaleka chivomezi panali moto; koma Yehova sanali m’motomo. Utaleka moto panali bata la kamphepo kayaziyazi.

13 Ndipo atamva Eliya, anafunda nkhope yake ndi chofunda chake, natuluka, naima pa khomo la phangalo. Ndipo taonani, anamdzera mau akunena naye, Uchitanji kuno, Eliya?

14 Nati iye, Ndachitira changu Yehova Mulungu wa makamu; popeza ana a Israele ataya chipangano chanu, nagumula maguwa la nsembe anu, napha aneneri anu ndi lupanga; ndipo ndatsala ndekha, ndipo afuna moyo wanga kuuchotsa.

15 Ndipo Yehova anati kwa iye, Bwerera ulendo wako, udzere kuchipululu kunka ku Damasiko, ndipo utafikako udzoze Hazaele akhale mfumu ya Aramu;

16 ukadzozenso Yehu mwana wa Nimisi akhale mfumu ya Israele; ukadzozenso Elisa mwana wa Safati wa ku Abele-Mehola akhalemnenerim’malo mwako.

17 Ndipo kudzachitika Yehu adzamupha amene adzapulumuka ku lupanga la Hazaele; ndi Elisa adzamupha amene adzapulumuka ku lupanga la Yehu.

18 Ndiponso ndidasiya mu Israele anthu zikwi zisanu ndi ziwiri osagwadiraBaalamaondo ao, osampsompsona ndi milomo yao.

19 Tsono anachokako, napeza Elisa mwana wa Safati alikukoketsa chikhasu ng’ombe ziwiriziwiri magoli khumi ndi awiri, iye yekha anakhala pa goli lakhumi ndi chiwiri; ndipo Eliya ananka kunali iyeyo, naponya chofunda chake pa iye.

20 Ndipo iye anasiya ng’ombe zija, namthamangira Eliya, nati, Ndiloleni ndiyambe ndakampsompsona atate wanga ndi amai wanga; nditatero ndidzakutsatani. Nati iye, Bwerera ndakuchitanji?

21 Ndipo anabwerera panali iye uja, natengako ng’ombe ziwiri, nazipha, naphikira nyama yake ndi zipangizo za zochitira nazo ng’ombe, napatsa anthu adye. Atatero, ananyamuka, natsata Eliya, namtumikira.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1KI/19-48172288e3b76673a661e5e4daa0369f.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *