Categories
1 ATESALONIKA

1 ATESALONIKA 2

Za utumiki wake wa kwa Atesalonika

1 Pakuti, abale, mudziwa nokha malowedwe athu a kwa inu, kuti sanakhale opanda pake;

2 koma tingakhale tidamva zowawa kale, ndipo anatichitira chipongwe, monga mudziwa, ku Filipi, tinalimbika pakamwa mwa Mulungu wathu kulankhula ndi inu Uthenga Wabwino wa Mulungu m’kutsutsana kwambiri.

3 Pakuti kudandaulira kwathu sikuchokera kukusochera, kapena kuchidetso, kapena m’chinyengo;

4 komatu monga Mulungu anativomereza kutiikiza Uthenga Wabwino, kotero tilankhula; osati monga okondweretsa anthu, koma Mulungu; amene ayesa mitima yathu.

5 Pakuti sitinayende nao mau osyasyalika nthawi iliyonse monga mudziwa, kapena kupsinjika msiriro, mboni ndi Mulungu;

6 kapena sitinakhale ofuna ulemerero wa kwa anthu, kapena kwa inu, kapena kwa ena, tingakhale tinali nayo mphamvu yakukulemetsani mongaatumwiaKhristu.

7 Komatu tinakhala ofatsa pakati pa inu, monga m’mene mlezi afukata ana ake a iye yekha;

8 kotero ife poliralira inu, tinavomera mokondwera kupereka kwa inu si Uthenga Wabwino wa Mulungu wokha, komanso moyo wathu, popeza mudakhala okondedwa kwa ife.

9 Pakuti mukumbukira, abale, chigwiritso chathu ndi chivuto chathu; pochita usiku ndi usana, kuti tingalemetse wina wa inu, tinalalikira kwa inu Uthenga Wabwino wa Mulungu.

10 Inu ndinu mboni, Mulungunso, kuti tinakhala oyera mtima ndi olungama ndi osalakwa kwa inu akukhulupirira;

11 monga mudziwa kuti tinachitira yense wa inu pa yekha, monga atate achitira ana ake a iye yekha,

12 ndi kukudandaulirani, ndi kukusangalatsani ndi kuchita umboni, kuti muyende koyenera Mulungu, amene akuitanani inu mulowe ufumu wake wa Iye yekha, ndi ulemerero.

13 Ndipo mwa ichinso ife tiyamika Mulungu kosalekeza, kuti, pakulandira mau a Uthenga wa Mulungu, simunawalandire monga mau a anthu, komatu monga momwe ali ndithu, mau a Mulungu, amenenso achita mwa inu okhulupirira.

14 Pakuti inu, abale, munayamba kukhala akutsanza aMipingoya Mulungu yokhala mu Yudeya mwa Khristu Yesu; popeza zomwezi mudazimva kowawa ndinunso pamanja pa a mtundu wanu wa inu nokha, monganso iwowa pa manja a Ayuda;

15 amene adaphanso Ambuye Yesu, ndi aneneri, natilondalonda ife, ndipo sakondweretsa Mulungu, natsutsana nao anthu onse;

16 natiletsa ife kuti tisalankhule ndi akunja kuti apulumutsidwe; kudzaza machimo ao nthawi zonse; koma mkwiyo wafika pa iwo kufikira chimaliziro.

Paulo alira kuonanso Atesalonika. Akondwera pa uthenga anabwera nao Timoteo

17 Koma ife, abale, angakhale adatichotsa kusiyana nanu kanthawi, osapenyana maso, koma kusiyana mtima ai, tinayesetsa koposa kuona nkhope yanu ndi chilakolako chachikulu;

18 chifukwa tinafuna kudza kwa inu, inedi Paulo ndatero kamodzi kapena kawiri; komaSatanaanatiletsa.

19 Pakuti chiyembekezo chathu, kapena chimwemwe, kapena korona wakudzitamandira naye nchiyani? Si ndinu nanga, pamaso pa Ambuye wathu Yesu m’kufika kwake?

20 Pakuti inu ndinu ulemerero wathu ndi chimwemwe chathu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1TH/2-5a950346687d3e302a2da49c9c780a4d.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *