1 Paulo, ndi Silivano, ndi Timoteo, kwaMpingowa Atesalonika mwa Mulungu Atate ndi Ambuye YesuKhristu:Chisomo kwa inu ndi mtendere.
Zipatso za Uthenga Wabwino ku Tesalonika
2 Tiyamika Mulungu nthawi zonse chifukwa cha inu nonse, ndi kukumbukira inu m’mapemphero athu;
3 ndi kukumbukira kosalekeza ntchito yanu ya chikhulupiriro, ndi chikondi chochitachita, ndi chipiriro cha chiyembekezo cha Ambuye wathu Yesu Khristu, pamaso pa Mulungu Atate wathu;
4 podziwa, abale okondedwa ndi Mulungu, chisankhidwe chanu,
5 kuti Uthenga Wabwino wathu sunadze kwa inu m’mau mokha, komatunso mumphamvu, ndi mwa Mzimu Woyera, ndi m’kuchuluka kwakukulu; monga mudziwa tinakhala onga otani mwa inu chifukwa cha inu.
6 Ndipo munayamba kukhala akutsanza athu, ndi a Ambuye, m’mene mudalandira mauwo m’chisautso chambiri, ndi chimwemwe cha Mzimu Woyera;
7 kotero kuti munayamba kukhala inu chitsanzo kwa onse akukhulupirira mu Masedoniya ndi muAkaya.
8 Pakuti kutuluka kwa inu kudamveka mau a Ambuye, osati mu Masedoniya ndi Akaya mokha, komatu m’malo monse chikhulupiriro chanu cha kwa Mulungu chidatuluka; kotero kuti sikufunika kwa ife kulankhula kanthu.
9 Pakuti iwo okha alalikira za ife, malowedwe athu a kwa inu anali otani; ndi kuti munatembenukira kwa Mulungu posiyana nao mafano, kutumikira Mulungu weniweni wamoyo,
10 ndi kulindirira Mwana wake achokere Kumwamba, amene anamuukitsa kwa akufa, Yesu, wotipulumutsa ife kumkwiyo ulinkudza.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1TH/1-0dcf0da58c93390180e7a1f4f31a65b7.mp3?version_id=1068—