Categories
1 AKORINTO

1 AKORINTO 5

Za chigololo mu Mpingo wa ku Korinto. Awadzudzulapo

1 Kwamveka ndithu kuti kuli chigololo pakati panu, ndipo chigololo chotere chonga sichimveka mwaamitundu, kuti wina ali naye mkazi wa atate wake.

2 Ndipo mukhala odzitukumula, kosati makamaka mwachita chisoni, kuti achotsedwe pakati pa inu iye amene anachita ntchito iyi.

3 Pakuti inedi, thupi langa kulibe, koma mzimu wanga ulipo, ndaweruza kale, monga ngati ndilipo,

4 m’dzina la Ambuye wathu Yesu, posonkhana pamodzi inu ndi mzimu wanga, ndi mphamvu ya Ambuye wathu Yesu,

5 kumpereka iye wochita chotere kwaSatana, kuti lionongeke thupi, kuti mzimu upulumutsidwe m’tsiku la Ambuye Yesu.

6 Kudzitamanda kwanu sikuli bwino. Kodi simudziwa kuti chotupitsa pang’ono chitupitsa mtanda wonse?

7 Tsukani chotupitsa chakale, kuti mukakhale mtanda watsopano, monga muli osatupa. PakutinsoPaskawathu waphedwa, ndiyeKhristu;

8 chifukwa chake tichita phwando, si ndi chotupitsa chakale, kapena ndi chotupitsa cha dumbo, ndi kuipa mtima, koma ndi mkate wosatupa wa kuona mtima, ndi choonadi.

9 Ndinalembera inu m’kalata ija, kuti musayanjane ndi achigololo;

10 si konsekonse ndi achigololo a dziko lino lapansi, kapena ndi osirira, ndi okwatula, kapena ndi opembedza mafano; pakuti nkutero mukatuluke m’dziko lapansi;

11 koma tsopano ndalembera inu kuti musayanjane naye, ngati wina wotchedwa mbale ali wachigololo, kapena wosirira, kapena wopembedza mafano, kapena wolalatira, kapena woledzera, kapena wolanda, kungakhale kukadya naye wotere, iai.

12 Pakuti nditani nao akunja kukaweruza iwo? Kodi amene ali m’katimo simuwaweruze ndi inu,

13 koma akunja awaweruza Mulungu? Chotsani woipayo pakati pa inu nokha.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1CO/5-8de96fb35045b32164ccac34373262e7.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *