Categories
1 AKORINTO

1 AKORINTO 12

Mphatso za Mzimu zisiyana

1 Koma za mphatso zauzimu, abale, sindifuna kuti mukhale osadziwa.

2 Mudziwa kuti pamene munaliamitundu, munatengedwa kunka kwa mafano aja osalankhula, monga munatsogozedwa.

3 Chifukwa chake ndikuuzani inu, kuti palibe munthu wakulankhula mwa Mzimu wa Mulungu, anena, Yesu ngwotembereredwa; ndipo palibe wina akhoza kunena, Yesu ali Ambuye, koma mwa Mzimu Woyera.

4 Ndipo pali mphatso zosiyana, koma Mzimu yemweyo.

5 Ndipo pali mautumiki osiyana, koma Ambuye yemweyo.

6 Ndipo pali machitidwe osiyana, koma Mulungu yemweyo, wakuchita zinthu zonse mwa onse.

7 Koma kwa yense kwapatsidwa maonekedwe a Mzimu kuti apindule nao.

8 Pakuti kwa mmodzi kwapatsidwa mwa Mzimu mau a nzeru; koma kwa mnzake mau a chidziwitso, monga mwa Mzimu yemweyo:

9 kwa wina chikhulupiriro, mwa Mzimu yemweyo; ndi kwa wina mphatso za machiritso, mwa Mzimu mmodziyo;

10 ndi kwa wina machitidwe a mphamvu; ndi kwa wina chinenero; ndi kwa wina chizindikiro cha mizimu; kwa wina malilime a mitundumitundu; ndi kwa wina mamasulidwe a malilime.

11 Koma zonse izi achita Mzimu mmodzi yemweyo, nagawira yense pa yekha monga afuna.

Thupi ndi limodzi, zingakhale ziwalo zisiyana

12 Pakuti monga thupi lili limodzi, nilikhala nazo ziwalo zambiri; koma ziwalo zonse za thupilo, pokhala zambiri, zili thupi limodzi; momwemonsoKhristu.

13 Pakutinso mwa Mzimu mmodzi ife tonse tinabatizidwa kulowa m’thupi limodzi, ngakhale Ayuda, ngakhale Agriki, ngakhale akapolo, ngakhale mfulu; ndipo tonse tinamwetsedwa Mzimu mmodzi.

14 Pakutinso thupi silikhala chiwalo chimodzi, koma zambiri.

15 Ngati phazi likati, Popeza sindili dzanja, sindili wa thupi; kodi silili la thupi chifukwa cha ichi?

16 Ndipo ngati khutu likati, Popeza sindili diso, sindili wa thupi; kodi silili la thupi chifukwa cha ichi?

17 Ngati thupi lonse likadakhala diso, kukadakhala kuti kununkhiza?

18 Koma tsopano, Mulungu anaika ziwalo zonsezo m’thupi, monga anafuna.

19 Koma ngati zonse zikadakhala chiwalo chimodzi, likadakhala kuti thupi?

20 Koma tsopano pali ziwalo zambiri, koma thupi limodzi.

21 Ndipo diso silingathe kunena kwa dzanja, Sindikufuna iwe, kapenanso mutu kwa mapazi, Sindikufunani inu.

22 Koma makamakatu ziwalozo zoyesedwa zofooka m’thupi, zifunika;

23 ndipo zimene tiziyesa zochepa ulemu m’thupi, pa izi tiika ulemu wochuluka woposa; ndi zinthu zosakoma zikhala nacho chokometsera choposa.

24 Koma zokoma zathu zilibe kusowa; koma Mulungu analumikizitsa thupi, napatsa ulemu wochuluka kwa chosowacho;

25 kuti kusakhale chisiyano m’thupi; koma kuti ziwalo zifanane ndi kusamalana china ndi chinzake.

26 Ndipo chingakhale chiwalo chimodzi chimva chowawa, ziwalo zonse zimva pamodzi; chingakhale chimodzi chilemekezedwa, ziwalo zonse zikondwera nacho pamodzi.

27 Koma inu ndinu thupi la Khristu, ndi ziwalo, yense pa yekha.

28 Ndipotu Mulungu anaika ena muMpingo, poyambaatumwi, achiwiri aneneri, achitatu aphunzitsi, pamenepo zozizwa, pomwepo mphatso za machiritso, mathandizo, maweruziro, malilime a mitundumitundu.

29 Kodi ali onse atumwi? Ali aneneri onse kodi? Ali aphunzitsi onse? Ali onse ochita zozizwa?

30 Ali nazo mphatso za machiritso onse kodi? Kodi onse alankhula ndi malilime? Kodi onse amasulira mau?

31 Koma funitsitsani mphatso zoposa. Ndipo ndikuonetsani njira yokoma yoposatu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/1CO/12-19cbda32c38bca83612cbbe29e58f93b.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *